Home Uncategorized ADMARC ili ndi board yatsopano

ADMARC ili ndi board yatsopano

by Blessings Melo
0 comments

Bungwe la boma logula, kusunga ndi kugulitsa chimanga la ADMARC tsopano lili ndi bodi yatsopano yoyendetsa bungweli.


Izi ndi malingana ndi chikalata chomwe watulutsa Peter Sambani, mkulu oyendetsa kampani za boma mdziko muno.


Malingana ndi Chikalatacho, Counsel Pempho Likongwe ndi yemwe wasankhidwa ngati wa pampando wa bodi imeneyi.


Ndipo wena omwe asankhidwa ngati ma membala a bodi imeneyi ndi monga Inkosi Msakambewa, Selia Msiska, Olivia Chaju Liwewe, Daniel Alfred Chatonya, komanso Alfred Tcherani.


Bodi yatsopanoyi inayamba kugwira ntchito zake kuyambira mwezi watha pa 26 mwezi watha wa March.
Pakali pano, Sambani mchikalatacho, wati boma lili ndi chikhulupiliro kuti bodi yatsopanoyi ithandiza kwambiri kupititsa patsogolo ntchito za ADMARC mdziko muno.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00