Home Uncategorized Boma lati lilemba ogwira ntchito za umoyo mdziko muno

Boma lati lilemba ogwira ntchito za umoyo mdziko muno

by Blessings Melo
0 comments

Boma lati lilemba ntchito ogwira ntchito za umoyo owonjezera mdziko muno.


Wafotokoza izi ndi nduna ya za umoyo Khumbize Kandondo Chiponda, pomwe dzulo amayankha mafunso kuchokera kwa aphungu aku nyumba ya malamulo.


Malingana ndi Chiponda, pa ntchitoyi, boma lilemba ogwira ntchito za umoyo okwana 6,700 kudzera mu ndondomeko ya chaka chino kufikira ya mawa, yomwe nyumbayi yavomereza sabata yatha.


Mwa ogwira ntchito za umoyowa ndi monga madotolo, anamwino ndi ma HAS.


Ndipo kuonjezera apo, ndunayi yati boma likhalanso likukweza pa ntchito omwe agwira ntchito za chipatala kwa nthawi yaitali mdziko muno.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00